Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Ahebri 8:13 - Buku Lopatulika

13 Pakunena Iye, Latsopano, anagugitsa loyambali. Koma chimene chilinkuguga ndi kusukuluka, chayandikira kukanganuka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Pakunena Iye, Latsopano, anagugitsa loyambali. Koma chimene chilinkuguga ndi kusukuluka, chayandikira kukanganuka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Pakunena mau oti, “Chipangano chatsopano”. Mulungu akunena kuti chipangano choyamba nchotha ntchito. Paja chinthu chimene chayamba kutha ntchito nkumakalamba, ndiye kuti chili pafupi kuzimirira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

Onani mutuwo Koperani




Ahebri 8:13
15 Mawu Ofanana  

Tukulani maso anu kumwamba, ndipo muyang'ane pansi padziko pakuti kumwamba kudzachoka ngati utsi, ndi dziko lidzatha ngati chofunda, ndipo iwo amene akhala m'menemo adzafa ngati njenjete; koma chipulumutso changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chilungamo changa sichidzachotsedwa.


Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.


Ndipo choteronso chikho, atatha mgonero, nanena, Chikho ichi ndi pangano latsopano m'mwazi wanga wothiridwa chifukwa cha inu.


Chikondi sichitha nthawi zonse, koma kapena zonenera zidzakhala chabe, kapena malilime adzaleka, kapena nzeru idzakhala chabe.


amenenso anatikwaniritsa ife tikhale atumiki a pangano latsopano; si la chilembo, koma la mzimu; pakuti chilembo chipha, koma mzimu uchititsa moyo.


Chifukwa chake ngati munthu aliyense ali mwa Khristu ali wolengedwa watsopano; zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano.


Iyo idzataika; komatu mukhalitsa; ndipo iyo yonse idzasuka monga malaya;


ndi kwa Yesu Nkhoswe ya chipangano chatsopano, ndi kwa mwazi wa kuwaza wakulankhula chokoma choposa mwazi wa Abele.


Momwemonso Yesu wakhala Nkhoswe ya pangano loposa.


Koma tsopano Iye walandira chitumikiro chomveka koposa, umonso ali Nkhoswe ya pangano labwino loposa, limene likhazikika pa malonjezano oposa.


Pakuti powatchulira iwo chifukwa, anena, Taonani, akudza masiku, anena Ambuye, Ndipo ndidzapangana pangano latsopano ndi nyumba ya Israele, ndi nyumba ya Yuda,


Ndipo mwa ichi ali Nkhoswe ya chipangano chatsopano, kotero kuti, popeza kudachitika imfa yakuombola zolakwa za pa chipangano choyamba, oitanidwawo akalandire lonjezano la zolowa zosatha.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa