Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Samueli 13:21 - Buku Lopatulika

21 Koma pamene mfumu Davide anamva zonsezi, anakwiya ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 Koma pamene mfumu Davide anamva zonsezi, anakwiya ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Davide atazimva zimenezi, adapsa nazo mtima zedi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 13:21
10 Mawu Ofanana  

Ndipo pakumva icho ana ake aamuna a Yakobo anabwera pochokera kudambo: amunawo ndipo anapwetekwa mtima, nakwiya kwambiri, chifukwa iyeyo anachita chopusa choipira Israele pakugona ndi mwana wamkazi wa Yakobo; ndicho chosayenera kuchita.


Ndipo panali pamene Israele anakhala m'dzikomo, Rubeni anamuka nagona ndi Biliha, mkazi wamng'ono wa atate wake: ndipo Israele anamva. Ana aamuna a Yakobo anali khumi ndi awiri:


Chifukwa chake tsono lupanga silidzachoka pa nyumba yako nthawi zonse, popeza unandipeputsa Ine, nudzitengera mkazi wa Uriya Muhiti akhale mkazi wako.


Pamenepo mkwiyo wa Davide unayaka ndithu pa munthuyo, nati kwa Natani, Pali Yehova, munthu amene anachita ichi, ayenera kumupha;


Ndipo Abisalomu mlongo wake ananena naye, Kodi mlongo wako Aminoni anali ndi iwe? Koma tsopano ukhale chete, mlongo wanga, iye ali mlongo wako; usavutika ndi chinthuchi. Chomwecho Tamara anakhala wounguluma m'nyumba ya Abisalomu mlongo wake.


Ndipo Abisalomu sanalankhule ndi Aminoni chabwino kapena choipa, pakuti Abisalomu anamuda Aminoni popeza adachepetsa mlongo wake Tamara.


Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m'dziko; kuduliratu onse akuchita zopanda pake kumzinda wa Yehova.


Nanga umaponderezeranji nsembe yanga ndi chopereka changa, zimene ndinalamulira m'mokhalamo mwanga; ndipo uchitira ana ako ulemu koposa Ine, kudzinenepetsa inu nokha ndi zokometsetsa za zopereka zao zonse za Aisraele, anthu anga?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa