Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Samueli 12:20 - Buku Lopatulika

20 Pamenepo Davide ananyamuka pansi, nasamba, nadzola, nasintha zovala; nafika kunyumba ya Yehova, napembedza; pamenepo anafika kunyumba yake; ndipo powauza anamuikira chakudya, nadya iye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Pamenepo Davide ananyamuka pansi, nasamba, nadzola, nasintha zovala; nafika kunyumba ya Yehova, napembedza; pamenepo anafika kunyumba yake; ndipo powauza anamuikira chakudya, nadya iye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Apo Davide adadzuka pansi paja, ndipo adakasamba, nadzola mafuta, nkusintha zovala zake. Tsono adakaloŵa m'nyumba ya Chauta, nakapembedza. Pambuyo pake adapita kunyumba kwake, naitanitsa chakudya. Ndipo anthu atabwera nacho, iye adadya.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 12:20
20 Mawu Ofanana  

Koma pamene Davide anaona anyamata ake likunong'onezana, Davide anazindikira kuti mwanayo adafa; Davide nanena ndi anyamata ake, Kodi mwanayo wafa? Nati iwo, Wafa.


Pamenepo anyamata ake ananena naye, Ichi mwachita nchiyani? Mwanayo akali moyo, munasala kudya ndi kumlira, koma pakufa mwanayo munyamuka ndi kudya.


Ndipo Yowabu anatumiza ku Tekowa, natenga kumeneko mkazi wanzeru, nanena naye, Ukokomezeke monga mfedwa, nuvale zovala za pamaliro, osadzola mafuta, koma ukhale ngati munthu wamkazi wakulira akufa nthawi yaikulu.


Ndipo Mefiboseti mwana wa Saulo anatsika kukakomana ndi mfumu; ndipo sadasambe mapazi ake, kapena kumeta ndevu zake, kapena kutsuka zovala zake kuyambira tsiku lomuka mfumu kufikira tsiku lobwera kwao mumtendere.


Ndipo pamene adalowa nalo likasa la Mulungu analiika pamalo pake pakati pa hema amene Davide adaliutsira; ndipo Davide anapereka nsembe zopsereza, ndi nsembe zoyamika pamaso pa Yehova.


Pomwepo Davide mfumu analowa, nakhala pansi pamaso pa Yehova; nati, Ine ndine yani, Yehova Mulungu, ndi banja langa ndi chiyani kuti munandifikitsa pano?


Pamenepo Yobu ananyamuka, nang'amba malaya ake, nameta mutu wake, nagwa pansi, nalambira,


Koma ananena naye, Ulankhula monga amalankhula akazi opusa. Ha! Tidzalandira zokoma kwa Mulungu kodi, osalandiranso zoipa? Pa ichi chonse Yobu sanachimwe ndi milomo yake.


Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.


Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo, wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.


Ndinakhala duu, sindinatsegule pakamwa panga; chifukwa inu mudachichita.


Tiyeni, tipembedze tiwerame; tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga.


Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;


Zovala zako zikhale zoyera masiku onse; mutu wako usasowe mafuta.


Koma iwe, posala kudya, dzola mutu wako, ndi kusamba nkhope yako:


Sunandidzoza mutu wanga ndi mafuta; koma uyu anadzoza mapazi anga ndi mafuta onunkhira bwino.


Usambe tsono, nudzole, nuvale zovala zako, nutsikire popunthirapo, koma usadziwike naye munthuyo, koma atatha kudya ndi kumwa ndiko.


Chifukwa chake tsono, mukhululukire tchimo langa, nimubwerere pamodzi ndi ine, kuti ndikalambire Yehova.


Chomwecho Samuele anabwerera natsata Saulo; ndi Saulo analambira Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa