Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Mbiri 4:1 - Buku Lopatulika

1 Anapanganso guwa la nsembe lamkuwa, m'litali mwake mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwake mikono makumi awiri, ndi msinkhu wake mikono khumi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Anapanganso guwa la nsembe lamkuwa, m'litali mwake mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwake mikono makumi awiri, ndi msinkhu wake mikono khumi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Solomoni adapanga guwa lamkuŵa, m'litali mwake mamita asanu ndi anai, m'mimba mwake asanu ndi anainso, ndipo msinkhu wake pafupi mamita anai ndi theka.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Solomoni anapanga guwa lamkuwa limene mulitali mwake linali mamita asanu ndi anayi, mulifupi mwakenso mamita asanu ndi anayi ndipo msinkhu wake unali mamita anayi ndi theka.

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 4:1
11 Mawu Ofanana  

Ndipo Solomoni anaimirira ku guwa la nsembe la Yehova pamaso pa msonkhano wonse wa Israele, natambasulira manja ake kumwamba, nati,


Tsiku lomwelo mfumu inapatulira Mulungu pakati pake pa bwalo la ku khomo la nyumba ya Yehova; pakuti pomwepo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe yaufa, ndi mafuta a nsembe zamtendere; popeza guwa la nsembe lamkuwa linali pamaso pa Yehova lidachepa kulandira nsembe zopsereza, ndi nsembe zaufa, ndi mafuta a nsembe zamtendere.


Ndipo chaka chimodzi Solomoni anapereka katatu nsembe zopsereza ndi zamtendere, paguwa la nsembe limene anammangira Yehova, nafukiza zonunkhira paguwa la nsembe pamaso pa Yehova, atatsiriza nyumbayo.


Guwa la nsembe lomwe lamkuwa, adalipanga Bezalele mwana wa Uri mwana wa Huri linali komweko, ku khomo la chihema cha Yehova; ndipo Solomoni ndi khamulo anafunako.


Ndipo pakumva Asa mau awa, ndi chinenero cha Odedi mneneriyo, analimbika mtima, nachotsa zonyansazo m'dziko lonse la Yuda ndi Benjamini, ndi m'mizinda adailanda ku mapiri a Efuremu; nakonza guwa la nsembe la Yehova lokhala pakhomo pachipinda cholowera cha nyumba ya Yehova.


Pamenepo analowa m'katimo kwa mfumu Hezekiya, nati, Tayeretsa nyumba yonse ya Yehova, ndi guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zake zonse, ndi gome la mkate woonekera, ndi zipangizo zake zonse.


Ndipo Solomoni anapatula pakati pake pa bwalo lili pakhomo pa nyumba ya Yehova; pakuti anapereka nsembe zopsereza, ndi mafuta a nsembe zoyamika pomwepo; popeza guwa la nsembe lamkuwa adalipanga Solomoni linachepa kulandira nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa, ndi mafuta.


Pamenepo Solomoni anapereka nsembe zopsereza kwa Yehova paguwa la nsembe la Yehova, limene adalimanga pakhomo pachipinda cholowera,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa