Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Akorinto 11:29 - Buku Lopatulika

29 Afooka ndani wosafooka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

29 Afooka ndani wosafooka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

29 Ndani ali wofooka, ine osakhala naye pamodzi m'kufooka kwakeko? Ndani amene mnzake amchimwitsa, ine osavutika mu mtima?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

29 Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?

Onani mutuwo Koperani




2 Akorinto 11:29
36 Mawu Ofanana  

Ndipo wodala iye amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.


Ophunzira ake anakumbukira kuti kunalembedwa, Changu cha pa nyumba yanu chandidya ine.


Kondwani nao iwo akukondwera; lirani nao akulira.


Ndipo ife amene tili olimba tiyenera kunyamula zofooka za opanda mphamvu, ndi kusadzikondweretsa tokha.


Nanga mulibe nyumba za kudyeramo ndi kumweramo? Kapena kodi munyoza Mpingo wa Mulungu, ndi kunyoza iwo amene alibe kanthu? Ndidzanena chiyani kwa inu? Kodi ndidzatama inu m'menemo? Sindikutamani.


Ndipo chingakhale chiwalo chimodzi chimva chowawa, ziwalo zonse zimva pamodzi; chingakhale chimodzi chilemekezedwa, ziwalo zonse zikondwera nacho pamodzi.


Wopusa iwe, chimene uchifesa wekha sichikhalitsidwanso chamoyo, ngati sichifa;


Chifukwa chake, ngati chakudya chikhumudwitsa mbale wanga, sindidzadya nyama kunthawi yonse, kuti ndingakhumudwitse mbale wanga.


Koma yang'anirani kuti ulamuliro wanu umene ungakhale chokhumudwitsa ofookawo.


Kwa ofooka ndinakhala ngati wofooka, kuti ndipindule ofooka. Ndakhala zonse kwa anthu onse, kuti paliponse ndikapulumutse ena.


Pakuti tikondwera, pamene ife tifooka ndi inu muli amphamvu; ichinso tipempherera, ndicho ungwiro wanu.


Komatu pamene ndinaona kuti sanalikuyenda koongoka, monga mwa choonadi cha Uthenga Wabwino, ndinati kwa Kefa pamaso pa onse, Ngati inu muli Myuda mutsata makhalidwe a amitundu, ndipo si a Ayuda, mukakamiza bwanji amitundu atsate makhalidwe a Ayuda?


Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse chilamulo cha Khristu.


Ndidziwa ntchito zako, ndi chilemetso chako ndi chipiriro chako ndi kuti sungathe kulola oipa, ndipo unayesa iwo amene adzitcha okha atumwi, osakhala atumwi, nuwapeza onama;


Komatu ndili nako kotsutsana ndi iwe, kuti ulola mkazi Yezebele, wodzitcha yekha mneneri; ndipo aphunzitsa, nasocheretsa akapolo anga, kuti achite chigololo ndi kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa