Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Samueli 25:18 - Buku Lopatulika

18 Pomwepo Abigaile anafulumira, natenga mikate mazana awiri, ndi zikopa ziwiri za vinyo, nkhosa zisanu zowotchaotcha, ndi miyeso isanu ya tirigu wokazinga, ndi nchinchi za mphesa zouma zana limodzi, ndi nchinchi za nkhuyu mazana awiri, naziika pa abulu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Pomwepo Abigaile anafulumira, natenga mikate mazana awiri, ndi zikopa ziwiri za vinyo, nkhosa zisanu zoochaocha, ndi miyeso isanu ya tirigu wokazinga, ndi nchinchi za mphesa zouma zana limodzi, ndi nchinchi za nkhuyu mazana awiri, naziika pa abulu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 Tsono mwamsanga Abigaile adatenga mitanda yabuledi 200, matumba achikopa aŵiri a vinyo, nkhosa zisanu zootcheratu, makilogramu 17 a tirigu wokazinga, nchinchi za mphesa zoumika 100, ndiponso makeke ankhuyu 200. Zonsezo adazisenzetsa abulu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 Ndipo Abigayeli sanataye nthawi. Iye anatenga malofu a buledi 200, matumba a chikopa awiri a vinyo, nkhosa zisanu zowotcheratu, makilogalamu 17 a tirigu wokazinga, makeke a mphesa zowuma 100, ndiponso makeke a nkhuyu 200, ndipo anazisenzetsa abulu.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 25:18
14 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene Davide anapitirira pang'ono pamutu paphiri, onani, Ziba mnyamata wa Mefiboseti anakomana naye, ali nao abulu awiri omanga mbereko, ndi pamenepo mitanda ya mikate mazana awiri, ndi nchinchi zamphesa zana limodzi, ndi zipatso za m'dzinja zana limodzi, ndi thumba la vinyo.


Ndiponso akuyandikizana nao mpaka Isakara ndi Zebuloni ndi Nafutali anabwera nao mkate osenzetsa abulu, ndi ngamira, ndi nyuru, ndi ng'ombe, zakudya zaufa, ndi nchinchi zankhuyu, ndi nchinchi zamphesa, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi ng'ombe, ndi nkhosa zochuluka; pakuti munali chimwemwe mu Israele.


Mtulo wa munthu umtsegulira njira, numfikitsa pamaso pa akulu.


Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo, ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.


Mkaziyo amchitira zabwino, si zoipa, masiku onse a moyo wake.


Fulumira kuyanjana ndi mnzako wamlandu, pamene uli naye panjira; kapena mnzako wamlandu angakupereke iwe kwa woweruza mlandu, ndi woweruzayo angapereke iwe kwa msilikali, nuponyedwe iwe m'nyumba yandende.


Ndipo Yese anati kwa Davide mwana wake, Uwatengere abale ako efa wa tirigu uyu wokazinga, ndi mikate iyi khumi, nuthamangire nazo kuzithando kwa abale ako;


Chifukwa chake tsono mudziwe ndi kulingalira chimene mudzachita; popeza anatsimikiza mtima kuchitira choipa mbuye wathu, ndi nyumba yake yonse; popeza iye ali woipa, ndipo munthu sakhoza kulankhula naye.


Pakuti ndithu, Pali Yehova Mulungu wa Israele, amene anandiletsa lero kusapweteka iwe, ukadapanda kufulumira kubwera kundichingamira, zoonadi sindikadasiyira Nabala kufikira kutacha kanthu konse, ngakhale mwana wamwamuna mmodzi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa