Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Samueli 18:14 - Buku Lopatulika

14 Ndipo Davide anakhala wochenjera m'mayendedwe ake onse; ndipo Yehova anali naye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Ndipo Davide anakhala wochenjera m'mayendedwe ake onse; ndipo Yehova anali naye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Ndipo ankapambana pa zonse zimene ankachita, chifukwa Chauta anali naye.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 18:14
18 Mawu Ofanana  

Woyang'anira m'kaidi sanayang'anire kanthu kalikonse kamene kanali m'manja a Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi iye; ndipo zimene anazichita, Yehova anazipindulitsa.


Ndipo Davide anakula chikulire chifukwa Yehova Mulungu wa makamu anali naye.


Ndipo Yehova anali naye, nachita iye mwanzeru kulikonse anamukako, napandukira mfumu ya Asiriya osamtumikira.


Ndipo anaika asilikali a boma mu Edomu; ndi Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.


Ndipo Davide anaika asilikali a boma mu Aramu wa Damasiko; ndi Aaramu anasanduka anthu a Davide, nabwera nazo mphatso. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.


Ndipo Yehova anali ndi Yehosafati, popeza anayenda m'njira zake zoyamba za kholo lake Davide, osafuna Abaala;


Ndidzachita mwanzeru m'njira yangwiro; mudzandidzera liti? Ndidzayenda m'nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.


Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.


ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulani inu; ndipo onani, Ine ndili pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira chimaliziro cha nthawi ya pansi pano.


chifukwa Ine ndili pamodzi ndi iwe, ndipo palibe munthu adzautsana ndi iwe kuti akuipse; chifukwa ndili nao anthu ambiri m'mzinda muno.


Potero Yehova anakhala ndi Yoswa; ndi mbiri yake inabuka m'dziko lonse.


Ndipo Yehova anali ndi Yuda, iye nawaingitsa a kumapiri, osaingitsa nzika za kuchigwa, popeza zinali nao magaleta achitsulo.


Ndipo zitakufikirani zizindikiro izi mudzachita monga mudzaona pochita, pakuti Mulungu ali nanu.


Ndipo mnyamata wake wina anayankha, nati, Taonani, ine ndaona mwana wa Yese wa ku Betelehemu, ndiye wanthetemya wodziwa kuimbira, ndipo ali wa mtima wolimba ndi woyenera nkhondo, ndiponso ali wochenjera manenedwe ake; ndiye munthu wokongola, ndipo Yehova ali naye.


Ndipo pamene Saulo anaona kuti analikukhala wochenjera ndithu anamuopa.


Ndipo kunalinso nkhondo; ndipo Davide anatuluka, nakamenyana ndi Afilisti, nawapha ndi maphedwe aakulu, ndipo iwo anamthawa iye.


Ndipo Samuele anakula, Yehova nakhala naye, osalola kuti mau ake amodzi apite pachabe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa