Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Akorinto 15:41 - Buku Lopatulika

41 Kuli ulemerero wa dzuwa, ndi ulemerero wina wa mwezi, ndi ulemerero wina wa nyenyezi; pakuti nyenyezi isiyana ndi nyenyezi mu ulemerero.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

41 Kuli ulemerero wa dzuwa, ndi ulemerero wina wa mwezi, ndi ulemerero wina wa nyenyezi; pakuti nyenyezi isiyana ndi nyenyezi m'ulemerero.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

41 Dzuŵa lili ndi kuŵala kwake, mwezi uli ndi kuŵala kwake kosiyana ndi kwa dzuŵa kuja, nyenyezinso zili ndi kuŵala kwake kosiyana ndi kwa zina zija. Ngakhale nyenyezizo zimasiyananso kuŵala kwake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

41 Dzuwa lili ndi ulemerero wake, ndipo pali ulemerero wina wa mwezi, palinso ulemerero winanso wa nyenyezi. Ulemerero wa nyenyezi ndi wosiyanasiyana.

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 15:41
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Mulungu anati, Pakhale zounikira pathambo la kumwamba, zakulekanitsa usana ndi usiku; zikhale zizindikiro ndi nyengo, ndi masiku, ndi zaka;


ngati ndalambira dzuwa lilikuwala, kapena mwezi ulikuyenda monyezimira;


Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,


Pompo mwezi udzanyazitsidwa, ndi dzuwa lidzakhala ndi manyazi, pakuti Yehova wa makamu adzalamulira chaulemerero m'phiri la Ziyoni, ndi mu Yerusalemu, ndi pamaso pa akuluakulu ake.


Ndipo anati kwa iyenso, Khala iwenso woweruza mizinda isanu.


Palinso matupi am'mwamba, ndi matupi apadziko: koma ulemerero wa lam'mwamba ndi wina, ndi ulemerero wa lapadziko ndi winanso.


Chomwechonso kudzakhala kuuka kwa akufa. Lifesedwa m'chivundi, liukitsidwa m'chisavundi;


ndi kuti mungakweze maso anu kupenya kumwamba, ndipo poona dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi, khamu lonse la kumwamba, munganyengedwe ndi kuzigwadira, ndi kuzitumikira, zimene Yehova Mulungu wanu anagawira mitundu yonse ya anthu pansi pa thambo lonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa