Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Akorinto 11:4 - Buku Lopatulika

4 Mwamuna yense woveka mutu, popemphera kapena ponenera, anyoza mutu wake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Mwamuna yense woveka mutu, popemphera kapena ponenera, anyoza mutu wake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Ngati mwamuna apemphera kapena kulalika mau a Mulungu, atavala kanthu kumutu, akunyoza mutu wake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo.

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 11:4
11 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide anakwera pa chikweza cha ku Azitona nakwera nalira misozi; ndipo anafunda mutu wake nayenda ndi mapazi osavala; ndi anthu onse amene anali naye anafunda munthu yense mutu wake ndipo anakwera, nalira misozi pokwerapo.


Ndipo mfumu inafunda nkhope yake, nilira ndi mau okweza, Mwana wanga Abisalomu, Abisalomu, mwana wanga, mwana.


Pakuti mwana wamwamuna apeputsa atate, mwana wamkazi aukira amake, mpongozi aukira mpongozi wake; adani ake a munthu ndiwo a m'nyumba yake.


Ndipo kunali aneneri ndi aphunzitsi ku Antiokeya mu Mpingo wa komweko, ndiwo Barnabasi, ndi Simeoni, wonenedwa Wakuda, ndi Lusio wa ku Kirene, Manaene woleredwa pamodzi ndi Herode chiwangacho, ndi Saulo.


Kodi ubadwidwe womwe sutiphunzitsa kuti ngati mwamuna aweta tsitsi chinyozetsa iye?


Koma mkazi yense wakupemphera, kapena kunenera, wovula mutu, anyoza mutu wake; pakuti kuli chimodzimodzi kumetedwa.


ndi kwa wina machitidwe a mphamvu; ndi kwa wina chinenero; ndi kwa wina chizindikiro cha mizimu; kwa wina malilime a mitundumitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.


Ndipotu Mulungu anaika ena mu Mpingo, poyamba atumwi, achiwiri aneneri, achitatu aphunzitsi, pamenepo zozizwa, pomwepo mphatso za machiritso, mathandizo, maweruziro, malilime a mitundumitundu.


Ndipo ndingakhale ndikhoza kunenera, ndipo ndingadziwe zinsinsi zonse, ndi nzeru zonse, ndipo ndingakhale ndili nacho chikhulupiriro chonse, kuti ndikasendeza mapiri, koma ndilibe chikondi, ndili chabe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa