Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Akorinto 10:3 - Buku Lopatulika

3 nadya onse chakudya chauzimu chimodzimodzi;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 nadya onse chakudya chauzimu chimodzimodzi;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Onse ankadya chakudya chauzimu chimodzimodzi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 10:3
9 Mawu Ofanana  

ndi mkate wochokera m'mwamba munawapatsa pa njala yao; ndi madzi otuluka m'thanthwe munawatulutsira pa ludzu lao, ndi kuwauza alowe, nalandire dziko limene mudakwezapo dzanja lanu kuwapatsa.


Munawapatsanso mzimu wanu wokoma kuwalangiza, ndipo simunawamane mana anu pakamwa pao; munawapatsanso madzi pa ludzu lao.


Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri, nawakhutitsa mkate wakumwamba.


Ndipo pamene ana a Israele anakaona, anati wina ndi mnzake, Nchiyani ichi? Pakuti sanadziwe ngati nchiyani. Ndipo Mose ananena nao, Ndiwo mkatewo Yehova wakupatsani ukhale chakudya chanu.


Ndipo ana a Israele anadya mana zaka makumi anai, kufikira atalowa dziko la midzi; anadya mana kufikira analowa malire a dziko la Kanani.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, ndidzavumbitsira inu mkate wodzera kumwamba; ndipo anthu azituluka ndi kuola muyeso wa tsiku pa tsiku lake, kuti ndiwayese, ngati ayenda m'chilamulo changa kapena iai.


Ndipo anakuchepetsani, nakumvetsani njala, nakudyetsani ndi mana, amene simunawadziwe, angakhale makolo anu sanawadziwe; kuti akudziwitseni kuti munthu sakhala wamoyo ndi mkate wokha, koma munthu akhala wamoyo ndi zonse zakutuluka m'kamwa mwa Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa