Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Akorinto 1:11 - Buku Lopatulika

11 Pakuti zinamveka kwa ine za inu, abale anga, ndi iwo a kwa Koloe, kuti pali makani pakati pa inu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Pakuti zinamveka kwa ine za inu, abale anga, ndi iwo a kwa Koloe, kuti pali makani pakati pa inu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Pakuti ena a m'banja la Koloe andifotokozera kuti pali kukangana pakati panu, abale anga.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu.

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 1:11
19 Mawu Ofanana  

Ndipo anauza Rebeka mau a Esau mwana wake wamkulu: ndipo iye anatumiza naitana Yakobo mwana wake wamng'ono, nati kwa iye, Taona, mkulu wako Esau, kunena za iwe, adzitonthoza yekha mtima wake kuti adzakupha iwe.


Mibadwo ya Yakobo ndi iyi; Yosefe anali wa zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri analinkudyetsa zoweta pamodzi ndi abale ake; ndipo anali mnyamata pamodzi ndi ana a Biliha, ndi ana aamuna a Zilipa, akazi a atate wake; ndipo Yosefe anamfotokozera atate wake mbiri yao yoipa.


Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.


Milomo ya wopusa ifikitsa makangano; ndipo m'kamwa mwake muputa kukwapulidwa.


Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti munene chimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m'chiweruziro chomwecho.


Koma ichi ndinena, kuti yense wa inu anena, Ine ndine wa Paulo; koma ine wa Apolo; koma ine wa Kefa; koma ine wa Khristu.


Pakutitu poyamba posonkhana inu mu Mpingo, ndimva kuti pakhala malekano mwa inu; ndipo ndivomereza penapo.


pakuti, pokhala pali nkhwidzi ndi ndeu pakati pa inu simuli athupi kodi, ndi kuyendayenda monga mwa munthu?


Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale chotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi, ukazitape, zodzikuza, mapokoso;


Koma ngati mulumana ndi kudyana, chenjerani mungaonongane.


kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,


Tisakhale odzikuza, outsana, akuchitirana njiru.


Chitani zonse kopanda madandaulo ndi makani,


iyeyo watukumuka, wosadziwa kanthu, koma ayalukira pa mafunso ndi makani a mau, kumene zichokerako njiru, ndeu, zamwano, mayerekezo oipa;


koma pewa mafunso opusa, ndi mawerengedwe a mibadwo, ndi ndeu, ndi makani a pamalamulo; pakuti sizipindulitsa, ndipo zili zachabe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa