Yoweli 1:6 - Buku Lopatulika Pakuti mtundu wadza, wakwerera dziko langa, wamphamvu wosawerengeka, mano ake akunga mano a mkango, nukhala nao mano a chibwano a mkango waukulu. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pakuti mtundu wadza, wakwerera dziko langa, wamphamvu wosawerengeka, mano ake akunga mano a mkango, nukhala nao mano achibwano a mkango waukulu. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Chikhamu cha dzombe chagwa m'dziko lathu nchamphamvu ndiponso chosaŵerengeka. Mano ake ali ngati a mkango wamphongo, zibwano zake ngati za mkango waukazi. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi. |
Pali mbadwo mano ao akunga malupanga, zibwano zao zikunga mipeni; kuti adye osauka kuwachotsa kudziko, ndi aumphawi kuwachotsa mwa anthu.
Padziko la anthu anga padzafika minga ndi lunguzi; inde pa nyumba zonse zokondwa, m'mzinda wokondwerera;
Ndipo iye adzapitapita kulowa mu Yuda; adzasefukira, napitirira; adzafikira m'khosi; ndi kutambasula kwa mapiko ake, kudzakwanira dziko lanu m'chitando mwake, inu Imanuele.
Sadzakhala m'dziko la Yehova; koma Efuremu adzabwerera kunka ku Ejipito; ndipo adzadya chakudya chodetsa mu Asiriya.
Ndipo ndidzakubwezerani zaka zidazidya dzombe, ndi chirimamine, ndi anoni, ndi chimbalanga, gulu langa lalikulu la nkhondo, limene ndinalitumiza pakati pa inu.