Obadiya 1:6 - Buku Lopatulika Ha! Za Esau zasanthulidwa; ha! Zobisika zake zafunidwa. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ha! Za Esau zasanthulidwa; ha! Zobisika zake zafunidwa. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Onani m'mene alisakazira dziko la Esau, ndi m'mene achifunkhira chuma chake chonse. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa! |
Makanda ao adzatswanyidwe pamaso pao; m'nyumba mwao mudzafunkhidwa, ndi akazi ao adzakakamizidwa.
ndipo ndidzakupatsa iwe chuma cha mumdima, ndi zolemera zobisika za m'malo am'tseri, kuti iwe udziwe kuti Ine ndine Yehova, amene ndikuitana iwe dzina lako, ndine Mulungu wa Israele.
Pakuti ndamvula Esau, ndamvundukula, sadzatha kubisala; mbeu zake zaonongeka, ndi abale ake, ndi anansi ake, ndipo palibe iye.
Lupanga lili pa akavalo ao, ndi pa magaleta ao, ndi pa anthu onse osakanizidwa amene ali pakati pake, ndipo adzakhala ngati akazi; lupanga lili pa chuma chake, ndipo chidzalandidwa.
Iye avumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.