Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 6:11 - Buku Lopatulika

ndipo wansembe akonze imodzi nsembe yauchimo, ndi ina nsembe yopsereza, namtetezere popeza anachimwa nao mtembowo; ndipo apatulire mutu wake tsiku lomwelo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo wansembe akonze imodzi nsembe yauchimo, ndi ina nsembe yopsereza, namtetezere popeza anachimwa nao mtembowo; ndipo apatulire mutu wake tsiku lomwelo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Wansembeyo apereke imodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, inayo ikhale ya nsembe yopsereza. Tsono amchitire mwambo wopepesera machimo ake, chifukwa adalakwa poyandikana ndi mtembo. Tsiku lomwelo aperekenso tsitsi lake kwa Chauta,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.

Onani mutuwo



Numeri 6:11
4 Mawu Ofanana  

Ndipo chuma chake chikapanda kufikira nkhosa, wochimwayo adze nayo kwa Yehova nsembe yake yopalamula, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri; imodzi ikhale ya nsembe yauchimo, ndi ina ya nsembe yopsereza.


Ndipo awapatulire Yehova masiku a kusala kwake, nadze nayo nkhosa yamphongo ya chaka chimodzi ikhale nsembe yopalamula; koma masiku adapitawa azikhala chabe, popeza anadetsa kusala kwake.