Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 36:8 - Buku Lopatulika

Ndipo mwana wamkazi yense wa mafuko a ana a Israele, wakukhala nacho cholowa, akwatibwe ndi wina wa banja la fuko la kholo lake, kuti ana a Israele akhale nacho yense cholowa cha makolo ake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo mwana wamkazi yense wa mafuko a ana a Israele, wakukhala nacho cholowa, akwatibwe ndi wina wa banja la fuko la kholo lake, kuti ana a Israele akhale nacho yense cholowa cha makolo ake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mkazi aliyense amene alandira choloŵa m'fuko lililonse la Aisraele, akwatiwe ndi ana a abale a bambo wao. Mwisraele aliyense adzalandira choloŵa cha makolo ake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.

Onani mutuwo



Numeri 36:8
2 Mawu Ofanana  

Nafa Eleazara wopanda ana aamuna, koma ana aakazi ndiwo; ndi asuweni ao ana a Kisi anawatenga akhale akazi ao.


Motero cholowa cha ana a Israele sichidzanka ku fuko ndi fuko, pakuti mafuko a ana a Israele adzamamatira lonse ku cholowa chakechake.