Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 2:9 - Buku Lopatulika

Ndinafika tsono kwa ziwanga za tsidya lino la mtsinje, ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Koma mfumu idatumiza apite nane akazembe a nkhondo, ndi apakavalo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndinafika tsono kwa ziwanga za tsidya lino la mtsinje, ndipo ndinawapatsa akalata a mfumu. Koma mfumu idatumiza apite nane akazembe a nkhondo, ndi apakavalo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho ndidanyamuka ulendo nkukafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate, ndipo ndidaŵapatsa makalata a mfumu aja. Monsemo nkuti mfumu itatumiza akulu ankhondo ndiponso anthu okwera pa akavalo, kuti atsakane nane.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.

Onani mutuwo



Nehemiya 2:9
2 Mawu Ofanana  

Pakuti ndinachita manyazi kupempha kwa mfumu gulu la asilikali, ndi apakavalo, kutithandiza pa adani panjira; popeza tidalankhula ndi mfumu kuti, Dzanja la Mulungu wathu likhalira mokoma onse akumfuna; koma mphamvu yake ndi mkwiyo wake zitsutsana nao onse akumsiya.


Ndinanenanso kwa mfumu, Chikakomera mfumu, indipatse makalata kwa ziwanga za tsidya lija la mtsinje, andilole ndipitirire mpaka ndifikira ku Yuda;