Popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye wa ambuye; Mulungu wamkulu, wamphamvu, ndi woopsa, wosasamalira nkhope za anthu, kapena kulandira chokometsera mlandu.
Masalimo 136:3 - Buku Lopatulika Yamikani Mbuye wa ambuye; pakuti chifundo chake nchosatha. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Yamikani Mbuye wa ambuye; pakuti chifundo chake nchosatha. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Thokozani Chauta woposa ambuye onse, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Yamikani Ambuye wa ambuye, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. |
Popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye wa ambuye; Mulungu wamkulu, wamphamvu, ndi woopsa, wosasamalira nkhope za anthu, kapena kulandira chokometsera mlandu.
limene adzalionetsa m'nyengo za Iye yekha, amene ali Mwini Mphamvu wodala ndi wayekha, ndiye Mfumu ya mafumu ndi Mbuye wa ambuye;
Iwo adzachita nkhondo pa Mwanawankhosa, ndipo Mwanawankhosa adzawagonjetsa, chifukwa ali Mbuye wa ambuye, ndi Mfumu ya mafumu; ndipo adzawalakanso iwo akukhala naye, oitanidwa, ndi osankhika ndi okhulupirika.
Ndipo ali nalo pa chovala chake ndi pa ntchafu yake dzina lolembedwa, MFUMU YA MAFUMU, NDI MBUYE WA AMBUYE.