Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 7:5 - Buku Lopatulika

pakuti akonda mtundu wathu, ndipo anatimangira ife sunagoge.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

pakuti akonda mtundu wathu, ndipo anatimangira ife sunagoge.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

chifukwa amaukonda mtundu wathu, mwakuti adatimangira nyumba yamapemphero.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

chifukwa amakonda mtundu wathu ndipo anatimangira sunagoge wathu.”

Onani mutuwo



Luka 7:5
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Hiramu mfumu ya ku Tiro anatuma anyamata ake kwa Solomoni, popeza anamva kuti adamdzoza mfumu m'malo mwa atate wake; pakuti Hiramu adakondana ndi Davide masiku onse.


Ndipo iwo, pakufika kwa Yesu, anampempha Iye koumirira, nati, Ayenera iye kuti mumchitire ichi;


Ndipo Yesu anapita nao. Ndipo pakufika Iye tsono pafupi pa nyumba yake, kenturiyo anatuma kwa Iye abwenzi ake, kunena naye, Ambuye, musadzivute; pakuti sindiyenera ine kuti mudzalowe pansi pa tsindwi langa;


Pakuti mwa Khristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu chikhulupiriro, chakuchititsa mwa chikondi.


Ife tidziwa kuti tachokera kutuluka muimfa kulowa m'moyo, chifukwa tikondana ndi abale. Iye amene sakonda akhala muimfa.