Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 1:5 - Buku Lopatulika

Masiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali munthu wansembe, dzina lake Zakariya, wa gulu la ansembe la Abiya; ndi mkazi wake wa ana aakazi a fuko la Aroni, dzina lake Elizabeti.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Masiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali munthu wansembe, dzina lake Zekariya, wa gulu la ansembe la Abiya; ndi mkazi wake wa ana akazi a fuko la Aroni, dzina lake Elizabeti.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pa nthaŵi imene Herode anali mfumu ya dziko la Yudeya, kunali wansembe wina, dzina lake Zakariya, wa gulu la ansembe la Abiya. Mkazi wake Elizabeti anali wa fuko la Aroni.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.

Onani mutuwo



Luka 1:5
7 Mawu Ofanana  

wachisanu ndi chiwiri Hakozi, wachisanu ndi chitatu Abiya,


Awa ndi malongosoledwe ao mu utumiki wao kulowa m'nyumba ya Yehova, monga mwa chiweruzo adawapatsa Aroni atate wao, monga Yehova Mulungu wa Israele anamlamulira.


wa Abiya, Zikiri; wa Miniyamini, wa Mowadiya, Pilitai;


Ido, Ginetoyi, Abiya,


Ndipo pa kubadwa kwake kwa Yesu mu Betelehemu wa Yudeya m'masiku a Herode mfumu, onani, Anzeru a kum'mawa anafika ku Yerusalemu,


Koma mngelo anati kwa iye, Usaope Zekariya, chifukwa kuti lamveka pemphero lako, ndipo mkazi wako Elizabeti adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yohane.


Ndipo atatha masiku awa, Elizabeti mkazi wake anaima; nadzibisa miyezi isanu, nati,