Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 40:16 - Buku Lopatulika

Pamene wophika mkate anaona kuti kumasulira kwake kunali kwabwino, iye anati kwa Yosefe, Inenso ndinalimkulota, ndipo, taonani, malichero atatu a mikate yoyera anali pamutu panga;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamene wophika mkate anaona kuti kumasulira kwake kunali kwabwino, iye anati kwa Yosefe, Inenso ndinalimkulota, ndipo, taonani, malichero atatu a mikate yoyera anali pamtu panga;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Wophika buledi uja nayenso adaona kuti tanthauzo la malotowo linali labwino, adauza Yosefe kuti, “Inenso ndinalota nditasenza nsengwa zitatu za buledi pamutu pangapa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mkulu wa opanga buledi ataona kuti Yosefe wapereka tanthauzo labwino, anati kwa Yosefe, “Inenso ndinalota nditasenza nsengwa zitatu za buledi.

Onani mutuwo



Genesis 40:16
3 Mawu Ofanana  

chifukwa kuti ndinabedwa ndithu m'dziko la Ahebri; ndiponso pano sindinachite kanthu kakundiikira ine m'dzenjemu.


m'lichero lapamwamba munali mikate ya Farao ya mitundumitundu; ndipo mbalame zinadya ya m'lichero la pamutu panga.