Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 4:13 - Buku Lopatulika

Ndipo Kaini anati kwa Yehova, Kulangidwa kwanga nkwakukulu kosapiririka.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Kaini anati kwa Yehova, Kulangidwa kwanga nkwakukulu kosapiririka.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kaini adauza Chauta kuti, “Chilango chimenechi nchopitirira mphamvu zanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.

Onani mutuwo



Genesis 4:13
7 Mawu Ofanana  

pamene udzalima panthaka siidzaperekanso kwa iwe mphamvu yake: udzakhala wothawathawa ndi woyendayenda padziko lapansi.


Taonani, mwandiingitsa ine lero lomwe padziko; ndi pankhope panu ndidzabisika; ndipo ndidzakhala wothawathawa ndi woyendayenda padziko lapansi; ndipo kudzatero kuti onse akundipeza adzandipha.


Sakhulupirira kuti adzatulukamo mumdima, koma kuti lupanga limlindira.


Wasenza choipa chako ndi zonyansa zako, ati Yehova.


nachitira mwano Mulungu wa mu Mwamba chifukwa cha zowawa zao ndi zilonda zao; ndipo sanalape ntchito zao.


Ndipo anatsika kumwamba matalala aakulu, lonse lolemera ngati talente, nagwa pa anthu; ndipo anthu anachitira Mulungu mwano chifukwa cha mliri wa matalala, pakuti mliri wake ndi waukulu ndithu.


Ndipo anatenthedwa anthu ndi kutentha kwakukulu; ndipo anachitira mwano dzina la Mulungu wokhala nao ulamuliro pa miliri iyi; ndipo sanalape kuti amchitire ulemu.