Ndipo anakhala m'chipululu cha Parani; ndipo amake anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Ejipito.
Genesis 34:4 - Buku Lopatulika Ndipo anati Sekemu kwa atate wake Hamori kuti, Munditengere ine mkazi uyo akhale mkazi wanga. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo anati Sekemu kwa atate wake Hamori kuti, Munditengere ine mkazi uyo akhale mkazi wanga. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Choncho adakauza bambo wake kuti, “Nditengereni namwaliyu kuti akhale mkazi wanga.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Choncho Sekemu anati kwa abambo ake Hamori, “Mundipezere mtsikana uyu kuti akhale mkazi wanga.” |
Ndipo anakhala m'chipululu cha Parani; ndipo amake anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Ejipito.
Ndipo mtima wake unakhumba Dina mwana wake wamkazi wa Yakobo, ndipo anamkonda namwaliyo, nanena momkopa namwaliyo.
Ndipo anamva Yakobo kuti anamuipitsa Dina, mwana wake wamkazi; ana ake aamuna anali ndi zoweta zake kudambo: ndipo Yakobo anakhala chete mpaka anafika iwo.
Ndipo ine, manyazi anga ndidzapita nao kuti? Ndipo iwenso udzakhala ngati wina wa zitsiru mu Israele. Chifukwa chake tsono ulankhule ndi mfumu; iyeyu sadzakukaniza ine.
tengani akazi, balani ana aamuna ndi aakazi; kwatitsani ana anu aamuna, patsani ananu aakazi kwa amuna, kuti abale ana aamuna ndi aakazi; kuti mubalane pamenepo musachepe.
Nakwera iye, nauza atate wake ndi amai wake, nati, Ndapenya mkazi mu Timna wa ana aakazi a Afilisti; ndipo tsono munditengere uyu akhale mkazi wanga.