Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 26:11 - Buku Lopatulika

Ndipo Abimeleki anauza anthu ake, nati, Aliyense amene akhudza mwamuna uyo kapena mkazi wake, zoonatu adzaphedwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Abimeleki anauza anthu ake, nati, Aliyense amene akhudza mwamuna uyo kapena mkazi wake, zoonatu adzaphedwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Abimeleki adalamula anthu ake onse kuti, “Musamuchite kanthu munthuyu pamodzi ndi mkazi wake yemwe. Wina aliyense akangotero, aphedwa.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho Abimeleki analamula anthu ake onse nati, “Aliyense amene avutitse munthu uyu pamodzi ndi mkazi wake adzaphedwa ndithu.”

Onani mutuwo



Genesis 26:11
5 Mawu Ofanana  

Ndipo Mulungu anati kwa iye m'kulota, Inde ndidziwa Ine, kuti wachita icho ndi mtima wangwiro, ndipo Inenso ndinakuletsa iwe kuti usandichimwire ine: chifukwa chake sindinakuloleze iwe kuti umkhudze mkaziyo.


Ndipo Isaki anabzala m'dzikomo, nalandira za makumi khumi chaka chimenecho; ndipo Yehova anamdalitsa iye.


Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga, musamachitira choipa aneneri anga.


Chomwecho wolowa kwa mkazi wa mnzake; womkhudzayo sadzapulumuka chilango.


Pakuti atero Yehova wa makamu: Utatha ulemererowo ananditumiza kwa amitundu amene anakufunkhani; pakuti iye wokhudza inu, akhudza mwana wa m'diso lake.