Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 38:12 - Buku Lopatulika

Ndi pa mbali ya kumadzulo panali nsalu zotchingira za mikono makumi asanu, nsichi zake khumi, ndi makamwa ake khumi; zokowera za nsichi ndi mitanda yake yasiliva.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndi pa mbali ya kumadzulo panali nsalu zochingira za mikono makumi asanu, nsichi zake khumi, ndi makamwa ake khumi; zokowera za nsichi ndi mitanda yake yasiliva.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pa mbali yakuzambwe panali nsalu zochingira, kutalika kwake mamita 23, ndi nsanamira zake khumi ndi masinde khumi. Ngoŵe zake ndiponso mitanda yake zinali zasiliva.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.

Onani mutuwo



Eksodo 38:12
3 Mawu Ofanana  

ndi nsichi zake makumi awiri, ndi makamwa ao makumi awiri akhale amkuwa; zokowera za nsichi ndi mitanda yake zikhale zasiliva.


Ndi pa mbali ya kumpoto mikono zana limodzi, nsichi zake makumi awiri, ndi makamwa ake makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsichi ndi mitanda yake yasiliva.


Ndi pa mbali ya kum'mawa, kum'mawa, mikono makumi asanu.