Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 36:7 - Buku Lopatulika

Popeza zipangizo zinakwanira ntchito yonse ichitike, zinatsalakonso.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Popeza zipangizo zinakwanira ntchito yonse ichitike, zinatsalakonso.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zimene anali atazisonkhanitsa zidachuluka kuposa zimene zinkafunika kuti amalize ntchitoyo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.

Onani mutuwo



Eksodo 36:7
3 Mawu Ofanana  

Tsiku lomwelo mfumu inapatulira Mulungu pakati pake pa bwalo la ku khomo la nyumba ya Yehova; pakuti pomwepo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe yaufa, ndi mafuta a nsembe zamtendere; popeza guwa la nsembe lamkuwa linali pamaso pa Yehova lidachepa kulandira nsembe zopsereza, ndi nsembe zaufa, ndi mafuta a nsembe zamtendere.


Ndipo Azariya wansembe wamkulu wa nyumba ya Zadoki anamyankha, nati, Chiyambire anthu anabwera nazo zopereka kunyumba ya Yehova, tadya, takhuta, ndipo zitatsalira zambiri; pakuti Yehova anadalitsa anthu ake; ndipo siuku kuchuluka kwa chotsala.


Ndipo Mose analamulira, ndipo anamveketsa mau mu chigono chonse, ndi kuti, Asaonjezere ntchito ya ku chopereka cha malo opatulika, ngakhale mwamuna ngakhale mkazi. Tero anawaletsa anthu asabwere nazo zina.