Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 28:7 - Buku Lopatulika

Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Idzakhale ndi tizikwewo tam'mapewa tiŵiri tosokerera ku nsonga zake ziŵiri, tomangira efodiyo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.

Onani mutuwo



Eksodo 28:7
5 Mawu Ofanana  

Koma nsonga zake ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'tsogolo mwake.


Naombe efodi ndi golide, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya mmisiri.


Ndipo mpango wa efodi, wokhala pamenepo, kuti ammange nao, ukhale wa chiombedwe chomwecho, ndi woombera kumodzi, wagolide, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.


Ndi nsonga zake ziwiri zina za maunyolo awiri opotawo anazimanga pa zoikamo ziwiri, nazimanga pa zapamapewa za efodi, m'tsogolo mwake.


Anapangira efodi zapamapewa zolumikizana; pansonga ziwirizo anamlumikiza.