Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 13:6 - Buku Lopatulika

Masiku asanu ndi awiri uzikadya mkate wopanda chotupitsa, ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri likhale la madyerero a Yehova;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Masiku asanu ndi awiri uzikadya mkate wopanda chotupitsa, ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri likhale la madyerero a Yehova;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pa masiku asanu ndi aŵiri, muzidzadya buledi wosafufumitsa, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiŵirilo pazidzakhala chikondwerero cha Chauta.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.

Onani mutuwo



Eksodo 13:6
6 Mawu Ofanana  

Ndipo ana a Israele opezeka mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa masiku asanu ndi awiri ndi chimwemwe chachikulu; ndi Alevi ndi ansembe analemekeza Yehova tsiku ndi tsiku ndi zoimbira zakuliritsa kwa Yehova.


Uzisunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa. Uzidya mkate wopanda chotupitsa masiku asanu ndi awiri, monga ndakuuza pa nthawi yonenedwa, m'mwezi wa Abibu; pakuti mwezi wa Abibu unatuluka mu Ejipito.


Koma mubwere nayo kwa Yehova nsembe yamoto masiku asanu ndi awiri; pa tsiku lachisanu ndi chiwiri pakhale msonkhano wopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena.


Masiku asanu ndi limodzi muzidya mkate wopanda chotupitsa; ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri ndilo loletsa, la Yehova Mulungu wanu; musamagwira ntchito pamenepo.


Ndipo m'mawa mwake atatha Paska, anadya tirigu wakhwimbi wa m'dziko, mikate yopanda chotupitsa ndi tirigu wokazinga tsiku lomwe lija.