Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 1:13 - Buku Lopatulika

Ndipo Aejipito anawagwiritsa ana a Israele ntchito yosautsa;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Aejipito anawagwiritsa ana a Israele ntchito yosautsa;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

ndipo ankaŵakakamiza mwankhalwe kugwira ntchito yaukapolo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.

Onani mutuwo



Eksodo 1:13
8 Mawu Ofanana  

Ndipo anati kwa Abramu, Dziwitsa ndithu kuti mbeu zako zidzakhala alendo m'dziko la eni, ndipo zidzatumikira iwo, ndipo iwo adzasautsa izo zaka mazana anai;


nalankhula nao monga mwa uphungu wa achinyamata, nati, Atate wanga analemeretsa goli lanu, koma ine ndidzaonjezerapo pa goli lanu; atate wanga anakukwapulani ndi zikoti, koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.


Ndipo tsopano, popeza atate wanga anakusenzetsani goli lolemera, ine ndidzaonjezerapo pa goli lanu; atate wanga anakukwapulani ndi zikoti, koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.


Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ake, kuti achite monyenga ndi atumiki ake.


nawawitsa moyo wao ndi ntchito yolimba, ya dothi ndi ya njerwa, ndi ntchito zonse za pabwalo, ntchito zao zonse zimene anawagwiritsa nzosautsa.


Monga mkango wobangula ndi chilombo choyendayenda, momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.


Usamamweruza momzunza; koma uope Mulungu wako.


Koma Yehova anakutengani, nakutulutsani m'ng'anjo yamoto, mu Ejipito, mukhale kwa Iye anthu a cholowa chake, monga mukhala lero lino.