Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 17:21 - Buku Lopatulika

Ndipo kunali, atapita iwo, ajawo anatuluka m'chitsime, nanka nauza mfumu Davide; nati kwa Davide, Nyamukani nimuoloke madzi msanga; pakuti Ahitofele anapangira zotere pa inu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo kunali, atapita iwo, ajawo anatuluka m'chitsime, namka nauza mfumu Davide; nati kwa Davide, Nyamukani nimuoloke madzi msanga; pakuti Ahitofele anapangira zotere pa inu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ankhondo aja atapita, anthuwo adatuluka m'chitsime muja, ndipo adakauza mfumu Davide kuti, “Nyamukani, muwoloke mtsinje mofulumira, popeza kuti Ahitofele walangiza anthu ake zokuthirani nkhondo.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”

Onani mutuwo



2 Samueli 17:21
3 Mawu Ofanana  

Pomwepo Davide ananyamuka ndi anthu onse amene anali naye, naoloka Yordani. Kutacha m'mawa sanasowe mmodzi wa iwo wosaoloka Yordani.


Onani, ndikadathawira kutali, ndikadagona m'chipululu.