Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 14:5 - Buku Lopatulika

Ndipo mfumuyo inanena naye, Usowanji? Iye nayankha, Zoonadi ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo mfumuyo inanena naye, Usowanji? Iye nayankha, Zoonadi ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mfumuyo idamufunsa kuti, “Chikukuvutani nchiyani, mai?” Mkaziyo adayankha kuti, “Ha! Munthune ndine mkazi wamasiye. Mwamuna wanga adafa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.

Onani mutuwo



2 Samueli 14:5
6 Mawu Ofanana  

Ndipo Mulungu anamva mau a mnyamatayo, ndi mthenga wa Mulungu anamuitana Hagara, ndi mau odzera kumwamba, nati kwa iye, Watani Hagara? Usaope; chifukwa Mulungu anamva mau a mnyamata kumene ali.


Ndipo mkazi anauka nachoka, navula chofunda chake, navala zovala zamasiye zake.


Ndipo pamene mkazi wa ku Tekowayo anati alankhule ndi mfumuyo, anagwa nkhope yake pansi, namlambira, nati, Ndithandizeni mfumu.


Ndipo mdzakazi wanu ndinali nao ana aamuna awiri, ndipo awiriwo analimbana kumunda, panalibe wina wakuwaletsa, koma wina anakantha mnzake namupha.