Chomwecho Aminoni anagona, nadzikokomeza alikudwala; ndipo pamene mfumu inadza kumuona, Aminoni anati kwa mfumuyo, Mulole Tamara mlongo wanga abwere ndi kundipangira timitanda tiwiri pamaso panga, kuti ndikadye cha m'manja mwake.
2 Samueli 13:7 - Buku Lopatulika Ndipo Davide anatumiza mau kwao kwa Tamara, kuti, Upite kunyumba ya mlongo wako Aminoni, numkonzere chakudya. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo Davide anatumiza mau kwao kwa Tamara, kuti, Upite kunyumba ya mlongo wako Aminoni, numkonzere chakudya. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Davide adatumiza mau kwa Tamara kuti, “Upite kunyumba kwa mbale wako Aminoni, ukamphikire chakudya.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.” |
Chomwecho Aminoni anagona, nadzikokomeza alikudwala; ndipo pamene mfumu inadza kumuona, Aminoni anati kwa mfumuyo, Mulole Tamara mlongo wanga abwere ndi kundipangira timitanda tiwiri pamaso panga, kuti ndikadye cha m'manja mwake.
Chomwecho Tamara anapita kunyumba ya mlongo wake Aminoni; ndipo iye anali chigonere. Ndipo anatenga ufa naukanda naumba timitanda pamaso pake, nakazinga timitandato.
Ndipo Davide anadzimangira nyumba m'mzinda mwake, nakonzeratu malo likasa la Mulungu, naliutsira hema.