Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 17:41 - Buku Lopatulika

Ndipo Mfilistiyo anadza, nayandikira kwa Davide; ndi wonyamula chikopa chake anamtsogolera.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Mfilistiyo anadza, nayandikira kwa Davide; ndi wonyamula chikopa chake anamtsogolera.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Mfilistiyo adayambapo kupita kumene kunali Davide, munthu wonyamula chishango ali patsogolo pake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tsono Mfilisiti uja anayambapo kupita kumene kunali Davide, mnyamata wonyamula zida zake za nkhondo ali patsogolo pake.

Onani mutuwo



1 Samueli 17:41
4 Mawu Ofanana  

Pamenepo Yehova anati kwa Yoswa, Tambasula nthungoyo ili m'dzanja lako iloze ku Ai, pakuti ndidzaupereka m'dzanja lako. Ndipo Yoswa anatambasula nthungoyo inali m'dzanja lake kuloza mzinda.


Natenga ndodo yake m'dzanja lake nadzisankhira miyala isanu yosalala ya mumtsinje, naiika m'thumba la kubusa, limene anali nalo ndilo chibete; ndi choponyera miyala chinali m'dzanja lake, momwemo anayandikira kwa Mfilistiyo.


Ndipo Mfilisti pakumwazamwaza maso, ndi kuona Davide, anampeputsa; popeza anali mnyamata chabe, wofiirira, ndi wa nkhope yokongola.


Ndipo mtengo wa mkondo wake unali ngati mtanda woombera nsalu; ndi mutu wa mkondowo unalemera ngati masekeli mazana asanu ndi limodzi a chitsulo; ndipo womnyamulira chikopa anamtsogolera.