Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 10:18 - Buku Lopatulika

nanena ndi ana a Israele, Atero Yehova, Mulungu wa Israele kuti, Ine ndinatulutsa Israele mu Ejipito, ndipo ndinakupulumutsani m'manja a Aejipito, ndi m'manja a maufumu onse anakusautsani;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

nanena ndi ana a Israele, Atero Yehova, Mulungu wa Israele kuti, Ine ndinatulutsa Israele m'Ejipito, ndipo ndinakupulumutsani m'manja a Aejipito, ndi m'manja a maufumu onse anakusautsani;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adauza Aisraele onse kuti, “Chauta, Mulungu wa Aisraele, akuti, ‘Ndidakutulutsani inu Aisraele ku dziko la Ejipito, ndipo ndidakupulumutsani kwa Aejipito ndi kwa mafumu onse amene ankakusautsani.’

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’

Onani mutuwo



1 Samueli 10:18
7 Mawu Ofanana  

Ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, amene ndinawatulutsa m'dziko la Ejipito, kuti ndikhale pakati pao. Ine ndine Yehova Mulungu wao.


Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kuchita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize chokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukira inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.


Ndipo mthenga wa Yehova anakwera kuchokera ku Giligala kunka ku Bokimu. Ndipo anati, Ndinakukweretsani kuchokera ku Ejipito, ndi kulowetsa inu m'dziko limene ndinalumbirira makolo anu; ndipo ndinati, Sindidzathyola chipangano changa nanu ku nthawi yonse;


Pamene Yakobo anafika ku Ejipito, ndi makolo anu anapemphera kwa Yehova, Yehova anatumiza Mose ndi Aroni, amene anatulutsa makolo anu mu Ejipito, nawakhalitsa pamalo pano.