Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Zekariya 3:3 - Buku Lopatulika

3 Koma Yoswa analikuvala nsalu zonyansa naima pamaso pa mthenga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Koma Yoswa analikuvala nsalu zonyansa naima pamaso pa mthenga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Yoswa anali atavala zovala zalitsiro, pa nthaŵi imene adaaima pamaso pa mngelo uja.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Tsono Yoswa anali atavala zovala zalitsiro pa nthawi imene anayima pamaso pa mngelo.

Onani mutuwo Koperani




Zekariya 3:3
12 Mawu Ofanana  

Pamenepo Zerubabele mwana wa Sealatiele, ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki, ananyamuka, nayamba kumanga nyumba ya Mulungu ili ku Yerusalemu, anali pamodzi nao aneneri a Mulungu akuwathandiza.


Yehova Mulungu wa Israele, Inu ndinu wolungama, popeza tinatsala opulumuka monga lero lino; taonani, tili pamaso panu m'kupalamula kwathu; pakuti palibe wakuima pamaso panu chifukwa cha ichi.


pamene Ambuye adzasambitsa litsiro la ana aakazi a Ziyoni, nadzatsuka mwazi wa Yerusalemu, kuchokera pakatipo, ndi mzimu wa chiweruziro, ndi mzimu wakutentha.


Inu mukomana ndi iye amene akondwerera, nachita chilungamo, iwo amene akumbukira Inu m'njira zanu; taonani Inu munakwiya, ndipo ife tinachimwa; takhala momwemo nthawi yambiri, kodi tidzapulumutsidwa?


Pakuti ife tonse takhala ngati wina amene ali wosakonzeka; ndi zolungama zathu zonse zili ngati chovala chodetsedwa; ndipo ife tonse tifota monga tsamba, ndi zoipa zathu zitiuluza monga mphepo.


Mulungu wanga, tcherani khutu, nimumvere, tsegulani maso anu, nimupenye zopasuka zathu, ndi mzinda udatchedwawo dzina lanu; pakuti dzina lanu; pakuti sititula mapembedzero athu pamaso panu, chifukwa cha ntchito zathu zolungama, koma chifukwa cha zifundo zanu zochuluka.


Pakuti akalowa m'sunagoge mwanu munthu wovala mphete yagolide, ndi chovala chokometsetsa, ndipo akalowanso munthu wosauka ndi chovala chodetsa;


koma ena muwapulumutse ndi kuwakwatula kumoto; koma ena muwachitire chifundo ndi mantha, nimudane naonso malaya ochitidwa mawanga ndi thupi.


Ndipo anampatsa iye avale bafuta wonyezimira woti mbuu; pakuti bafuta ndiye zolungama za oyera mtima.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa