Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 3:8 - Buku Lopatulika

8 Onetsani inu zipatso zakuyenera kutembenuka mtima:

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Onetsani inu zipatso zakuyenera kutembenuka mtima:

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Chitanitu ntchito zosonyeza kuti mwatembenukadi mtima.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Onetsani chipatso cha kutembenuka mtima.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 3:8
16 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake tsopano konzani njira zanu ndi machitidwe anu, ndi kumvera mau a Yehova Mulungu wanu; ndipo Yehova adzaleka choipa chimene ananenera inu.


Kapena nyumba ya Yuda idzamva choipa chonse chimene nditi ndidzawachitire; kuti abwerere yense kuleka njira yake yoipa; kuti ndikhululukire mphulupulu yao ndi tchimo lao.


Popeza Yohane anadza kwa inu m'njira ya chilungamo, ndipo simunamvere iye; koma amisonkho ndi akazi achiwerewere anammvera iye; ndipo inu, m'mene munachiona, simunalape pambuyo pake, kuti mumvere iye.


Chifukwa chake balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tili naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.


komatu kuyambira kwa iwo a mu Damasiko, ndi a mu Yerusalemu, ndi m'dziko lonse la Yudeya, ndi kwa amitundunso ndinalalikira kuti alape, natembenukire kwa Mulungu, ndi kuchita ntchito zoyenera kutembenuka mtima.


pakuti kale munali mdima, koma tsopano muli kuunika mwa Ambuye; yendani monga ana a kuunika,


pakuti chipatso cha kuunika tichipeza mu ubwino wonse, ndi chilungamo, ndi choonadi,


odzala nacho chipatso cha chilungamo, chimene chili mwa Yesu Khristu, kuchitira Mulungu ulemerero ndi chiyamiko.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa