Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Marko 2:1 - Buku Lopatulika

1 Ndipo polowanso Iye mu Kapernao atapita masiku ena, kunamveka kuti ali m'nyumba.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ndipo polowanso Iye m'Kapernao atapita masiku ena, kunamveka kuti ali m'nyumba.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Patapita masiku pang'ono, Yesu adabwereranso ku Kapernao, anthu nkumva kuti ali kunyumba kwao.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.

Onani mutuwo Koperani




Marko 2:1
13 Mawu Ofanana  

ndipo anachoka ku Nazarete nadza nakhalitsa Iye mu Kapernao wa pambali pa nyanja, m'malire a Zebuloni ndi Nafutali:


Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumzinda kwao.


Koma iye anatuluka nayamba kulalikira ndithu, ndi kubukitsa mauwo, kotero kuti Yesu sanathe kulowanso poyera m'mudzi, koma anakhala padera m'mapululu; ndipo anadza kwa Iye anthu a kumalo onse.


Ndipo ambiri anaunjikana, kotero kuti anasowa malo, ngakhale pakhomo pomwe; ndipo analankhula nao mau.


Ndipo anthu ambiri anasonkhananso, kotero kuti sanathe iwo konse kudya.


Ndipo m'mene Iye adalowa m'nyumba kusiyana ndi khamulo, ophunzira ake anamfunsa Iye fanizolo.


Ndipo Iye anauka nachoka kumeneko, nanka ku maiko a ku Tiro ndi Sidoni. Ndipo analowa m'nyumba, nafuna kuti asadziwe anthu; ndipo sanakhoze kubisika.


Ndipo pamene Iye adalowa m'nyumba, ophunzira ake anamfunsa m'tseri, kuti, Nanga bwanji sitinathe ife kuutulutsa?


Ndipo anati kwa iwo, Kwenikweni mudzati kwa Ine nkhani iyi, Sing'anga iwe, tadzichiritsa wekha: zonse zija tazimva zinachitidwa ku Kapernao, muzichitenso zomwezo kwanu kuno.


Ndipo onani, anthu alikunyamulira pakama munthu wamanjenje; nafunafuna kulowa naye, ndi kumuika pamaso pa Iye.


Iyeyu, pamene anamva kuti Yesu wachokera ku Yudeya nafika ku Galileya, ananka kwa Iye, nampempha kuti atsike kukachiritsa mwana wake; pakuti anali pafupi imfa.


Koma pochitika mau awa, unyinji wa anthu unasonkhana, nusokonezedwa, popeza yense anawamva alikulankhula m'chilankhulidwe chake cha iye yekha.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa