Malaki 2:6 - Buku Lopatulika6 Chilamulo cha zoona chinali m'kamwa mwake, ndi chosalungama sichinapezeke m'milomo mwake; anayenda nane mumtendere ndi moongoka, nabweza ambiri aleke mphulupulu. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20146 Chilamulo cha zoona chinali m'kamwa mwake, ndi chosalungama sichinapezeka m'milomo mwake; anayenda nane mumtendere ndi moongoka, nabweza ambiri aleke mphulupulu. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa6 Malangizo amene ankapereka anali oona, pakamwa pao sipankatuluka zosalungama. Ankamvana nane, ndipo ankayenda mokhulupirika ndi Ine, motero ankabweza anthu ambiri m'njira zao zoipa. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero6 Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo. Onani mutuwo |