Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 6:11 - Buku Lopatulika

11 Koma iwowo anagwidwa misala; nalankhulana wina ndi mnzake kuti amchitire Yesu chiyani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Koma iwowo anagwidwa misala; nalankhulana wina ndi mnzake kuti amchitire Yesu chiyani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Koma akuluakulu aja adakwiya kwambiri, nayamba kukambirana zoti achite naye Yesu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Koma iwo anapsa mtima nayamba kukambirana wina ndi mnzake chomwe akanamuchitira Yesu.

Onani mutuwo Koperani




Luka 6:11
16 Mawu Ofanana  

Ichi ndi choipa m'zonse zichitidwa pansi pano, chakuti kanthu kamodzi kagwera onse; indetu, mtimanso wa ana a anthu wadzala udyo, ndipo misala ili m'mtima wao akali ndi moyo, ndi pamenepo apita kwa akufa.


Ndipo iwo anafunsana wina ndi mnzake, nati, Sitinatenge mikate.


Ndipo ansembe aakulu ndi Afarisi, pakumva mafanizo ake, anazindikira kuti alikunena za iwo.


Ndipo onse a m'sunagogemo anadzala ndi mkwiyo pakumva izi;


Ndipo pamene anaunguzaunguza pa iwo onse, anati kwa iye, Tansa dzanja lako. Ndipo iye anatero, ndi dzanja lake linabwerera momwe.


Ndipo kunali masiku awa, Iye anatuluka nanka kuphiri kukapemphera; nachezera usiku wonse m'kupemphera kwa Mulungu.


Pamenepo ansembe aakulu ndi Afarisi anasonkhanitsa akulu, nanena, Titani ife? Chifukwa munthu uyu achita zizindikiro zambiri.


Ndipo zitapita izi Yesu anayendayenda mu Galileya; pakuti sanafune kuyendayenda mu Yudeya, chifukwa Ayuda anafuna kumupha Iye.


Ndipo ndinawalanga kawirikawiri m'masunagoge onse, ndi kuwakakamiza anene zamwano; ndipo pakupsa mtima kwakukulu pa iwo ndinawalondalonda ndi kuwatsata ngakhale kufikira kumizinda yakunja.


Koma pamene anawalamulira iwo achoke m'bwalo la akulu a milandu, ananena wina ndi mnzake,


Koma Petro ndi Yohane anayankha nati kwa iwo, Weruzani, ngati nkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu;


Koma m'mene anamva iwo analaswa mtima, nafuna kuwapha.


Koma pakumva izi analaswa mtima, namkukutira mano.


Koma sadzapitirirapo; pakuti kupusa kwao kudzaonekeratu kwa onse, monganso kupusa kwa iwo aja.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa