Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 16:14 - Buku Lopatulika

14 Koma Afarisi, ndiwo okonda ndalama, anamva izi zonse; ndipo anamseka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Koma Afarisi, ndiwo okonda ndalama, anamva izi zonse; ndipo anamseka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Afarisi atamva zonsezi, adamseka Yesu, chifukwa iwo anali okonda ndalama.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.

Onani mutuwo Koperani




Luka 16:14
18 Mawu Ofanana  

Odzikuza anandinyoza kwambiri: koma sindinapatukanso nacho chilamulo chanu.


Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.


Inde agalu ali osusuka, sakhuta konse; amenewa ali abusa osazindikira; iwo onse atembenukira kunjira zao, yense kutsata phindu lake m'dera lake.


Pakuti kuyambira wamng'ono kufikira wamkulu onse akhala akusirira; ndiponso kuyambira mneneri kufikira wansembe onse achita monyenga.


Chifukwa chake ndidzapereka akazi ao kwa ena, ndi minda yao kwa iwo adzalowamo; pakuti onse kuyambira wamng'ono kufikira wamkulu asirirasirira; kuyambira mneneri kufikira wansembe onse achita zonyenga.


Ndipo akudzera monga amadzera anthu, nakhala pansi pamaso pako ngati anthu anga, namva mau ako, koma osawachita; pakuti pakamwa pao anena mwachikondi, koma mtima wao utsata phindu lao.


Koma tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mutsekera anthu Ufumu wa Kumwamba pamaso pao; pakuti inu nokha simulowamo, ndipo muwaletsa amene alikulowa, kuti asalowemo.


ananena, Tulukani, pakuti kabuthuko sikanafe koma kali m'tulo. Ndipo anamseka Iye pwepwete.


Ndipo Iye anati kwa iwo, Yang'anirani, mudzisungire kupewa msiriro uliwonse; chifukwa moyo wake wa munthu sulingana ndi kuchuluka kwa zinthu zake ali nazo.


amene aononga nyumba za akazi amasiye, ndipo monyenga achita mapemphero aatali; amenewo adzalandira kulanga koposa.


Ndipo anthu anaima alikupenya. Ndi akulunso anamlalatira Iye, nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Khristu wa Mulungu, wosankhidwa wake.


Ndipo anamseka Iye pwepwete podziwa kuti anafa.


Pakuti anthu adzakhala odzikonda okha, okonda ndalama, odzitamandira, odzikuza, amwano, osamvera akuwabala, osayamika,


kuti akalandire kuuka koposa; koma ena anayesedwa ndi matonzo ndi zokwapulira, ndiponso nsinga, ndi kuwatsekera m'ndende;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa