Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 16:16 - Buku Lopatulika

16 Ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi chimodzi, pamene Hagara anambalira Abramu Ismaele.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi chimodzi, pamene Hagara anambalira Abramu Ismaele.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Abramu anali wa zake 86 pa nthaŵi imeneyo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 16:16
7 Mawu Ofanana  

Ndipo anamuka Abramu monga Yehova ananena kwa iye, ndipo Loti anamuka pamodzi naye: ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi awiri kudza zisanu, pamene anatuluka mu Harani.


Ndipo Hagara anambalira Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anatcha dzina la mwana wake amene anambalira iye Hagara, Ismaele.


Ndipo Sarai mkazi wake wa Abramu anatenga Hagara mdzakazi wake wa ku Ejipito, Abramu atakhala m'dziko la Kanani zaka khumi, nampereka iye kwa Abramu mwamuna wake, kuti akhale mkazi wake.


Pamene Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi anai kudza zisanu ndi zinai, Yehova anamuonekera Abramu nati kwa iye, Ine ndine Mulungu Wamphamvuyonse; yenda iwe pamaso panga, nukhale wangwiro.


Ndipo Ismaele mwana wake anali wa zaka khumi ndi zitatu pamene anadulidwa m'khungu lake.


Ndipo Abrahamu anali wa zaka zana limodzi pamene anambadwira iye Isaki mwana wake.


Zaka za moyo wa Ismaele ndi izi: zaka zana limodzi kudza makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri: ndipo iye anamwalira, natengedwa akhale ndi a mtundu wake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa