Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 35:34 - Buku Lopatulika

34 Ndipo anaika m'mtima mwake kuti alangize ena, iye ndi Oholiyabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

34 Ndipo anaika m'mtima mwake kuti alangize ena, iye ndi Oholiyabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

34 Tsono Chauta wapatsa nzeru kwa iyeyo ndi kwa Oholiyabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, kuti aziphunzitsa ena luso laolo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 35:34
10 Mawu Ofanana  

ndiye mwana wa munthu wamkazi wa ana aakazi a Dani, ndipo atate wake ndiye munthu wa ku Tiro, wodziwa kuchita ndi golide, ndi siliva, ndi mkuwa, ndi chitsulo, ndi mwala, ndi mitengo, ndi thonje lofiirira, ndi lamadzi, ndi bafuta la thonje losansitsa ndi lofiira, ndi kuzokota mazokotedwe ali onse, ndi kulingirira chopanga chilichonse; kuti ampatse pokhala pamodzi ndi aluso anu, ndi aluso a mbuye wanga Davide atate wanu.


Pakuti Ezara adaikiratu mtima wake kuchifuna chilamulo cha Yehova, ndi kuchichita, ndi kuphunzitsa mu Israele malemba ndi maweruzo.


Wodala Yehova Mulungu wa makolo athu, amene anaika chinthu chotere mu mtima wa mfumu, kukometsera nyumba ya Yehova ili ku Yerusalemu,


Ndipo ndinauka usiku, ine ndi amuna owerengeka nane, osauza munthu yense ine choika Mulungu wanga m'mtima mwanga ndichitire Yerusalemu; panalibenso nyama ina nane, koma nyama imene ndinakhalapo.


Ndipo Ine, taona, ndampatsa Oholiyabu, mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, akhale naye; ndipo ndaika luso m'mitima ya onse a mtima waluso, kuti apange zonse ndakuuza iwe;


ndi kuzokota miyala yoikika, ndi kuzokota mitengo, kuchita m'ntchito zilizonse zaluso.


Koma kwa yense kwapatsidwa maonekedwe a Mzimu kuti apindule nao.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa