Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Aefeso 5:1 - Buku Lopatulika

1 Chifukwa chake khalani akutsanza a Mulungu, monga ana okondedwa;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Chifukwa chake khalani akutsanza a Mulungu, monga ana okondedwa;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Tsono popeza kuti ndinu ana okondedwa a Mulungu, muziyesa kumtsanzira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu.

Onani mutuwo Koperani




Aefeso 5:1
13 Mawu Ofanana  

Kodi Efuremu ndiye mwana wanga wokondedwa? Kodi ndiye mwana wokondweretsa? Nthawi zonse zoti ndimnenera zomtsutsa, pakuti ndimkumbukiranso ndithu; chifukwa chake mumtima mwanga ndimlirira; ndidzamchitiradi chifundo, ati Yehova.


Angakhale anatero, kuwerenga kwake kwa ana a Israele kudzanga mchenga wa kunyanja, wosayeseka kapena kuwerengeka; ndipo kudzatero kuti m'mene adawanena, Simuli anthu anga, adzanena nao, Muli ana a Mulungu wamoyo.


Pakuti Ine ndine Yehova amene ndinakukwezani kukutulutsani m'dziko la Ejipito, ndikhale Mulungu wanu; chifukwa chake mukhale oyera, popeza Ine ndine woyera.


kotero kuti mukakhale ana a Atate wanu wa Kumwamba; chifukwa Iye amakwezera dzuwa lake pa oipa ndi pa abwino, namavumbitsira mvula pa olungama ndi pa osalungama.


Chifukwa chake inu mukhale angwiro, monga Atate wanu wa Kumwamba ali wangwiro.


Koma onse amene anamlandira Iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lake;


Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.


kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda chilema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,


Chifukwa chake valani, monga osankhika a Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa, mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, kuleza mtima;


Okondedwa, ngati Mulungu anatikonda ife kotero, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa