Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Samueli 5:4 - Buku Lopatulika

4 Davide anali ndi zaka makumi atatu polowa iye ufumu wake, nakhala mfumu zaka makumi anai.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Davide anali ndi zaka makumi atatu polowa iye ufumu wake, nakhala mfumu zaka makumi anai.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Davide anali wa zaka makumi atatu za kubadwa pamene adaloŵa ufumu. Adakhala mu ufumu zaka makumi anai.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 5:4
7 Mawu Ofanana  

Ndipo Yosefe anali wa zaka makumi atatu pamene iye anaima pamaso pa Farao mfumu ya Aejipito. Ndipo Yosefe anatuluka pamaso pa Farao, napitapita padziko lonse la Ejipito.


Ndipo masiku ake akukhala Davide mfumu ya Israele anali zaka makumi anai; zaka zisanu ndi ziwiri anakhala mfumu ku Hebroni, ndi zaka makumi atatu mphambu zitatu anakhala mfumu ku Yerusalemu.


Yeriya ndiye mkulu wa Ahebroni, wa Ahebroni monga mwa mibadwo ya nyumba za makolo. Chaka cha makumi anai cha ufumu wa Davide anafunafuna, napeza mwa iwowa ngwazi zamphamvu ku Yazere wa ku Giliyadi.


Ndipo nthawi yoti anakhala mfumu ya Israele ndiyo zaka makumi anai; zaka zisanu ndi ziwiri anakhala mfumu mu Hebroni, ndi zaka makumi atatu anakhala mfumu mu Yerusalemu.


Anambadwira asanu ndi mmodzi mu Hebroni; ndi pomwepo anakhala mfumu zaka zisanu ndi ziwiri, ndi miyezi isanu ndi iwiri; ndi mu Yerusalemu anakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zitatu.


kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire ntchito ya chihema chokomanako.


Ndipo Yesuyo, pamene anayamba ntchito yake, anali monga wa zaka makumi atatu, ndiye (monga anthu adamuyesa) mwana wa Yosefe, mwana wa Eli,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa