Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 8:13 - Buku Lopatulika

Ndipo Yehova anachita monga mwa mau a Mose; nafa achulewo kuchokera m'zinyumba, ndi m'mabwalo, ndi m'minda.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yehova anachita monga mwa mau a Mose; nafa achulewo kuchokera m'zinyumba, ndi m'mabwalo, ndi m'minda.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Chauta adachitadi monga momwe Mose adapemphera. Motero achule onse aja amene adaali m'nyumba, pa bwalo ndi m'minda momwe, adafa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa

Onani mutuwo



Eksodo 8:13
6 Mawu Ofanana  

Pakuti ntchito yao ndiyo kuimirira ana a Aroni, atumikire m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo, ndi kuzipinda, ndi kuyeretsa zopatulika zonse; inde ntchito za utumiki wa nyumba ya Mulungu;


Ananena, ndipo inadza mitambo ya ntchentche, ndi nsabwe kufikira m'malire ao onse.


Ndipo achule adzachokera inu, ndi nyumba zanu, ndi anyamata anu, ndi anthu anu; adzatsala m'mtsinje mokha.


Ndipo Mose ndi Aroni anatuluka kwa Farao; ndi Mose anafuulira kwa Yehova kunena za achule amene adawaika pa Farao.


Ndipo anawaola miulumiulu; ndi dziko linanunkha.