Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 23:30 - Buku Lopatulika

Ndidzawaingitsa pang'onopang'ono pamaso pako, kufikira utachuluka, ndi kulandira dziko cholowa chako.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndidzawaingitsa pang'onopang'ono pamaso pako, kufikira utachuluka, ndi kulandira dziko cholowa chako.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ndidzaŵapirikitsa pang'onopang'ono, mpaka mutabala ana ambiri amene angathe kutenga dzikolo,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.

Onani mutuwo



Eksodo 23:30
5 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova Mulungu wanu adzataya amitundu awa pang'onopang'ono; simuyenera kuwaononga msanga, kuti zingakuchulukireni zilombo.


nzika zonse za kumapiri kuyambira Lebanoni, mpaka Misirefoti-Maimu, Asidoni onse; ndidzawainga pamaso pa ana a Israele, koma limeneli uwagawire Aisraele, likhale cholowa chao, monga ndinakulamulira.


Taonani, ndakugawirani mitundu ya anthu iyi yotsala ikhale cholowa cha mafuko anu, kuyambira ku Yordani, ndi mitundu yonse ya anthu ndinaipasula, mpaka ku Nyanja Yaikulu ku malowero a dzuwa.


Ndipo Yehova Mulungu wanu Iyeyu adzawapirikitsa pamaso panu, ndi kulanda dziko lao kuwachotsa pamaso panu, ndipo mudzalandira dziko lao likhale cholowa chanu; monga Yehova Mulungu wanu ananena ndi inu.


Pakuti Yehova anaingitsa pamaso panu mitundu yaikulu ndi yamphamvu; koma inu, palibe munthu anaima pamaso panu mpaka lero lino.