Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 6:11 - Buku Lopatulika

Ndipo likasa la Yehova linakhala m'nyumba ya Obededomu Mgiti miyezi itatu; ndipo Yehova anadalitsa Obededomu ndi banja lake lonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo likasa la Yehova linakhala m'nyumba ya Obededomu Mgiti miyezi itatu; ndipo Yehova anadalitsa Obededomu ndi banja lake lonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho Bokosi lachipanganolo lidakhala miyezi itatu m'nyumba ya Obededomu wa ku Gati. Ndipo Chauta adadalitsa Obededomu ndi banja lake lonse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Bokosi la Yehova linakhala mʼnyumba ya Obedi-Edomu Mgiti kwa miyezi itatu, ndipo Yehova anamudalitsa kwambiri iyeyo ndi banja lake lonse.

Onani mutuwo



2 Samueli 6:11
7 Mawu Ofanana  

Ndipo Labani anati kwa iye, Ngatitu ndikapeza ufulu pamaso pako, ukhale, chifukwa ndazindikira kuti Yehova wandidalitsa ine chifukwa cha iwe.


Woyang'anira m'kaidi sanayang'anire kanthu kalikonse kamene kanali m'manja a Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi iye; ndipo zimene anazichita, Yehova anazipindulitsa.


Ndipo panali chiyambire anamuyesa iye woyang'anira pa nyumba yake, ndi pa zake zonse, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwejipito chifukwa cha Yosefe; ndipo mdalitso wa Yehova unali pa zake zonse, m'nyumba ndi m'munda.


Momwemo Davide sanafune kudzitengera likasa la Yehova lidze kumzinda wa Davide; koma Davide analipambutsira kunyumba ya Obededomu Mgiti.


Ndipo Obededomu anali nao ana, woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinai Sakara, wachisanu Netanele,


Mubwere nalo limodzilimodzi lonse la khumi, kunyumba yosungiramo, kuti m'nyumba mwanga mukhale chakudya; ndipo mundiyese nako tsono, ati Yehova wa makamu, ngati sindikutsegulirani mazenera a kumwamba, ndi kukutsanulirani mdalitso wakuti adzasoweka malo akuulandira.