Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 17:19 - Buku Lopatulika

Ndipo mkazi anatenga chivundikiro nachiika pakamwa pa chitsime, napapasapo lipande la tirigu; momwemo sichinadziwike.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo mkazi anatenga chivundikiro nachiika pakamwa pa chitsime, napapasapo lipande la tirigu; momwemo sichinadziwika.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono mkazi wa munthu uja adatenga chivundikiro, nachiika pamwamba pa chitsimecho, nkuyanikapo tirigu, kotero kuti chitsimecho sichinkadziŵika.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.

Onani mutuwo



2 Samueli 17:19
3 Mawu Ofanana  

Ndipo anamwino ananena ndi Farao, Popeza akazi a Ahebri safanana ndi akazi a Aejipito; pakuti ali ndi mphamvu, naona ana asanafike anamwino.


Ndipo Mose anatuluka kwa Farao m'mzinda nakweza manja ake kwa Yehova; ndipo mabingu ndi matalala analeka, ndi mvula siinavumbanso padziko.