Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 13:30 - Buku Lopatulika

Ndipo kunali akali panjira, mau anafika kwa Davide, kuti, Abisalomu anapha ana aamuna onse a mfumu, osatsalapo ndi mmodzi yense.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo kunali akali panjira, mau anafika kwa Davide, kuti, Abisalomu anapha ana amuna onse a mfumu, osatsalapo ndi mmodzi yense.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma anthuwo akali m'njira, Davide adamva mphekesera zakuti Abisalomu wapha ana onse aamuna a mfumu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsalako.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”

Onani mutuwo



2 Samueli 13:30
3 Mawu Ofanana  

Ndipo anyamata a Abisalomu anamchitira Aminoni monga umo Abisalomu anawalamulira. Pomwepo ana aamuna onse a mfumu ananyamuka, nakwera munthu yense pa nyuru yake, nathawa.


Pamenepo mfumu inanyamuka ning'amba zovala zake nigona pansi, ndipo anyamata ake onse anaimirirapo ndi zovala zao zong'ambika.


Ndipo kunali, pakumuona anang'amba zovala zake, nati, Tsoka ine, mwana wanga, wandiweramitsa kwakukulu, ndiwe wa iwo akundisaukitsa ine; pakuti ndamtsegulira Yehova pakamwa panga ine, ndipo sinditha kubwerera.