Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Obadiya 1:16 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

16 Pakuti monga munamwa paphiri langa lopatulika, momwemo amitundu onse adzamwa kosalekeza; inde adzamwa, nadzameza, nadzakhala monga ngati sanalipo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Pakuti monga munamwa pa phiri langa lopatulika, momwemo amitundu onse adzamwa kosalekeza; inde adzamwa, nadzameza, nadzakhala monga ngati sanalipo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Anthu anga adamwa chikho cha zoŵaŵa pa phiri langa loyera, koma mitundu ina ya anthu idzamwa chikho cha zoŵaŵa kopitirira. Idzachita kugugudiza chikhocho kenaka nkuzimirira pomwepo.

Onani mutuwo Koperani




Obadiya 1:16
13 Mawu Ofanana  

Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.


Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.


Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.


“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.


onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.


Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa