Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 7:14 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

14 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Adaperekanso kambale kamodzi kagolide kolemera magaramu 110, kodzaza ndi lubani.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 7:14
13 Mawu Ofanana  

mbale zagolide weniweni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, mbale ndi zofukizira; ndiponso zomangira zitseko zagolide za chipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndiponso za zitseko za chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu.


Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.


zozimitsira nyale zagolide weniweni, mbale zowazira magazi, mbale ndi zofukizira; ndiponso zitseko zagolide za Nyumba ya Mulungu, chitseko cha ku Malo Opatulika Kwambiri ndi zitseko za ku chipinda chachikulu.


mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;


Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.


“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.


Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;


mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;


Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;


mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa